Job 6 (BOGWICC)

1 Tsono Yobu anayankha kuti, 2 “Achikhala mavuto anga anayezedwa,ndipo zipsinjo zanga zonse zikanayikidwa pa sikelo! 3 Ndithu, zikanalemera kupambana mchenga wa ku nyanja;nʼchifukwa chake mawu anga akhala okhadzula. 4 Mivi ya Wamphamvuzonse yandibaya,thupi langa likumva ululu wa miviyo;zoopsa za Mulungu zandizinga. 5 Kodi bulu wakuthengo amalira akakhala ndi msipu,nanga ngʼombe imalira ikakhala ndi chakudya? 6 Kodi chakudya chosakoma nʼkuchidya chopanda mchere,nanga choyera cha dzira chimakoma? 7 Zakudya zimenezi sindifuna nʼkuzilawa komwe;zakudya zimenezi zimabwerera kukhosi. 8 “Aa, ndikanalandira chimene ndikuchipempha,chikhala Mulungu anandipatsa chimene ndikuchiyembekezera, 9 achikhala chinamukomera Mulungu kuti anditswanye,kulola dzanja lake kuti lindimenye ndi kundiwonongeratu! 10 Pamenepo ine ndikanakhalabe ndi chitonthozo ichi,ndikanakondwa mu ululu wanga wosalekezawupodziwa kuti sindinakane mawu a Woyerayo. 11 “Kodi mphamvu zanga nʼzotani kuti ndizikhalabe ndi chiyembekezo?Nanga zoyembekezera zanga nʼzotani kuti ndipirirebe? 12 Kodi ine ndili ndi mphamvu?Nanga thupi langa ndi lolimba ngati chitsulo? 13 Kodi ndili ndi mphamvu zodzithandizira ndekha,nanga pakuti thandizo lachotsedwa kwa ine? 14 “Munthu amene ali kakasi ayenera kukhala ndi abwenzi odzipereka,ngakhale kuti iyeyo wasiya kuopa Wamphamvuzonse. 15 Koma abale anga ndi wosadalirika ngati mitsinje yowuma msanga,ngati mitsinje imene imathamanga. 16 Ali ngati mitsinje ya madzi akuda nthawi ya dzinja,imene madzi ake amakhala ambiri chifukwa chakuchuluka kwa mvula, 17 koma madziwo amasiya kuyenda nthawi yachilimwe,ndipo nthawi yotentha madziwo amawumiratu mʼmitsinjemo. 18 Anthu oyenda pa ngamira amapatukirako kufuna madzi;iwo amangoyendayenda nʼkufera mʼchipululu. 19 Anthu oyenda pa ngamira a ku Tema amafunafuna madzi,anthu amalonda apaulendo a ku Seba amafunafuna mwa chiyembekezo. 20 Amataya mtima chifukwa ankayembekezera kupeza madzi;koma akafika kumeneko, amangokhumudwako. 21 Tsono inunso mukuonetsa kuti ndinu osathandiza,mukuona chinthu choopsa kwambiri ndipo mukuchita mantha. 22 Kodi ine ndinanenapo kuti, ‘Ndiperekereni kenakake,ndilipirireni dipo kuchokera pa chuma chanu, 23 ndilanditseni mʼdzanja la mdani,ndiwomboleni mʼdzanja la munthu wankhanza?’ 24 “Phunzitseni, ndipo ine ndidzakhala chete;ndionetseni pomwe ndalakwitsa. 25 Ndithu, mawu owona ndi opweteka!Koma mawu anu otsutsa akufuna kuonetsa chiyani? 26 Kodi inu mukufuna kundidzudzula pa zimene ndikunena,ndipo mukufuna kuyesa mawu a munthu wosweka mtima ngati mphepo chabe? 27 Inu mungathe kuchita maere kuti mugulitse ana amasiyendi kumugulitsa bwenzi lanu. 28 “Koma tsopano ndichitireni chifundo pamene mukundiyangʼana.Kodi ine ndingayankhule zabodza pamaso panu? 29 Fewani mtima, musachite zosalungama;ganiziraninso popeza chilungamo changa chikanalipobe. 30 Kodi pali choyipa chilichonse pa milomo yanga?Kodi pakamwa panga sipangathe kuzindikira kanthu koyipa?

In Other Versions

Job 6 in the ANGEFD

Job 6 in the ANTPNG2D

Job 6 in the AS21

Job 6 in the BAGH

Job 6 in the BBPNG

Job 6 in the BBT1E

Job 6 in the BDS

Job 6 in the BEV

Job 6 in the BHAD

Job 6 in the BIB

Job 6 in the BLPT

Job 6 in the BNT

Job 6 in the BNTABOOT

Job 6 in the BNTLV

Job 6 in the BOATCB

Job 6 in the BOATCB2

Job 6 in the BOBCV

Job 6 in the BOCNT

Job 6 in the BOECS

Job 6 in the BOHCB

Job 6 in the BOHCV

Job 6 in the BOHLNT

Job 6 in the BOHNTLTAL

Job 6 in the BOICB

Job 6 in the BOILNTAP

Job 6 in the BOITCV

Job 6 in the BOKCV

Job 6 in the BOKCV2

Job 6 in the BOKHWOG

Job 6 in the BOKSSV

Job 6 in the BOLCB

Job 6 in the BOLCB2

Job 6 in the BOMCV

Job 6 in the BONAV

Job 6 in the BONCB

Job 6 in the BONLT

Job 6 in the BONUT2

Job 6 in the BOPLNT

Job 6 in the BOSCB

Job 6 in the BOSNC

Job 6 in the BOTLNT

Job 6 in the BOVCB

Job 6 in the BOYCB

Job 6 in the BPBB

Job 6 in the BPH

Job 6 in the BSB

Job 6 in the CCB

Job 6 in the CUV

Job 6 in the CUVS

Job 6 in the DBT

Job 6 in the DGDNT

Job 6 in the DHNT

Job 6 in the DNT

Job 6 in the ELBE

Job 6 in the EMTV

Job 6 in the ESV

Job 6 in the FBV

Job 6 in the FEB

Job 6 in the GGMNT

Job 6 in the GNT

Job 6 in the HARY

Job 6 in the HNT

Job 6 in the IRVA

Job 6 in the IRVB

Job 6 in the IRVG

Job 6 in the IRVH

Job 6 in the IRVK

Job 6 in the IRVM

Job 6 in the IRVM2

Job 6 in the IRVO

Job 6 in the IRVP

Job 6 in the IRVT

Job 6 in the IRVT2

Job 6 in the IRVU

Job 6 in the ISVN

Job 6 in the JSNT

Job 6 in the KAPI

Job 6 in the KBT1ETNIK

Job 6 in the KBV

Job 6 in the KJV

Job 6 in the KNFD

Job 6 in the LBA

Job 6 in the LBLA

Job 6 in the LNT

Job 6 in the LSV

Job 6 in the MAAL

Job 6 in the MBV

Job 6 in the MBV2

Job 6 in the MHNT

Job 6 in the MKNFD

Job 6 in the MNG

Job 6 in the MNT

Job 6 in the MNT2

Job 6 in the MRS1T

Job 6 in the NAA

Job 6 in the NASB

Job 6 in the NBLA

Job 6 in the NBS

Job 6 in the NBVTP

Job 6 in the NET2

Job 6 in the NIV11

Job 6 in the NNT

Job 6 in the NNT2

Job 6 in the NNT3

Job 6 in the PDDPT

Job 6 in the PFNT

Job 6 in the RMNT

Job 6 in the SBIAS

Job 6 in the SBIBS

Job 6 in the SBIBS2

Job 6 in the SBICS

Job 6 in the SBIDS

Job 6 in the SBIGS

Job 6 in the SBIHS

Job 6 in the SBIIS

Job 6 in the SBIIS2

Job 6 in the SBIIS3

Job 6 in the SBIKS

Job 6 in the SBIKS2

Job 6 in the SBIMS

Job 6 in the SBIOS

Job 6 in the SBIPS

Job 6 in the SBISS

Job 6 in the SBITS

Job 6 in the SBITS2

Job 6 in the SBITS3

Job 6 in the SBITS4

Job 6 in the SBIUS

Job 6 in the SBIVS

Job 6 in the SBT

Job 6 in the SBT1E

Job 6 in the SCHL

Job 6 in the SNT

Job 6 in the SUSU

Job 6 in the SUSU2

Job 6 in the SYNO

Job 6 in the TBIAOTANT

Job 6 in the TBT1E

Job 6 in the TBT1E2

Job 6 in the TFTIP

Job 6 in the TFTU

Job 6 in the TGNTATF3T

Job 6 in the THAI

Job 6 in the TNFD

Job 6 in the TNT

Job 6 in the TNTIK

Job 6 in the TNTIL

Job 6 in the TNTIN

Job 6 in the TNTIP

Job 6 in the TNTIZ

Job 6 in the TOMA

Job 6 in the TTENT

Job 6 in the UBG

Job 6 in the UGV

Job 6 in the UGV2

Job 6 in the UGV3

Job 6 in the VBL

Job 6 in the VDCC

Job 6 in the YALU

Job 6 in the YAPE

Job 6 in the YBVTP

Job 6 in the ZBP